< Masalimo 135 >
1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Alleluia. Louez le nom de Yahweh, louez-le, serviteurs de Yahweh,
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
vous qui êtes de service dans la maison de Yahweh, dans les parvis de la maison de notre Dieu.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Louez Yahweh, car Yahweh est bon; chantez son nom sur la harpe, car il est plein de douceur.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
Car Yahweh s’est choisi Jacob, il s’est choisi Israël pour en faire son héritage.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Oui, je le sais, Yahweh est grand, notre Seigneur est au-dessus de tous les dieux.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Tout ce que veut Yahweh, il le fait, dans les cieux et sur la terre, dans la mer et dans tous les abîmes.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
Il fait monter les nuages des extrémités de la terre, il produit les éclairs avec la pluie, il tire le vent de ses trésors.
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
Il frappa jadis les premiers-nés de l’Égypte, depuis l’homme jusqu’à l’animal.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
Il fit éclater des signes et des prodiges au milieu de toi, ô Égypte, contre Pharaon et tous ses serviteurs.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Il frappa des nations nombreuses, et fit mourir des rois puissants:
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Séhon, roi des Amorrhéens, Og, roi de Basan, et tous les rois de Canaan.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
Et il donna leur pays en héritage, en héritage à Israël, son peuple.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Yahweh, ton nom subsiste à jamais; Yahweh, ton souvenir dure d’âge en âge.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
Car Yahweh fait droit à son peuple, et il a compassion de ses serviteurs.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Les idoles des nations sont de l’argent et de l’or, ouvrage de la main des hommes.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Elles ont une bouche et ne parlent pas; elles ont des yeux et ne voient pas.
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
Elles ont des oreilles et n’entendent pas; Il n’y a pas même un souffle dans leur bouche.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Qu’ils leur ressemblent ceux qui les font, quiconque se confie en elles!
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Maison d’Israël, bénissez Yahweh! Maison d’Aaron, bénissez Yahweh!
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Maison de Lévi, bénissez Yahweh! Vous qui craignez Yahweh, bénissez Yahweh!
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Que de Sion soit béni Yahweh, qui habite Jérusalem! Alleluia!