< Masalimo 135 >
1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Alleluya. Herie ye the name of the Lord; ye seruauntis of the Lord, herie ye.
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
Ye that stonden in the hous of the Lord; in the hallis of `the hous of oure God.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Herie ye the Lord, for the Lord is good; singe ye to his name, for it is swete.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
For the Lord chees Jacob to him silf; Israel in to possessioun to him silf.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
For Y haue knowe, that the Lord is greet; and oure God bifore alle goddis.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
The Lord made alle thingis, what euere thingis he wolde, in heuene and in erthe; in the see, and in alle depthis of watris.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
He ledde out cloudis fro the ferthest part of erthe; and made leitis in to reyn. Which bringith forth wyndis fro hise tresours;
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
which killide the firste gendrid thingis of Egipt, fro man `til to beeste.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
He sente out signes and grete wondris, in the myddil of thee, thou Egipt; in to Farao and in to alle hise seruauntis.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Which smoot many folkis; and killide stronge kingis.
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Seon, the king of Ammorreis, and Og, the king of Basan; and alle the rewmes of Chanaan.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
And he yaf the lond of hem eritage; eritage to Israel, his puple.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Lord, thi name is with outen ende; Lord, thi memorial be in generacioun and in to generacioun.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
For the Lord schal deme his puple; and he schal be preied in hise seruauntis.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
The symulacris of hethene men ben siluer and gold; the werkis of the hondis of men.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Tho han a mouth, and schulen not speke; tho han iyen, and schulen not se.
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
Tho han eeris, and schulen not here; for `nether spirit is in the mouth of tho.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Thei that maken tho, be maad lijk tho; and alle that tristen in tho.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
The hous of Israel, blesse ye the Lord; the hous of Aaron, blesse ye the Lord.
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
The hous of Leuy, blesse ye the Lord; ye that dreden the Lord, `blesse ye the Lord.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Blessid be the Lord of Syon; that dwellith in Jerusalem.