< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Praise ye the name of the Lord: O you his servants, praise the Lord:
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
You that stand in the house of the Lord, in the courts of the house of our God.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Praise ye the Lord, for the Lord is good: sing ye to his name, for it is sweet.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
For the Lord hath chosen Jacob unto himself: Israel for his own possession.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
For I have known that the Lord is great, and our God is above all gods.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Whatsoever the Lord hath pleased he hath done, in heaven, in earth, in the sea, and in all the deeps.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
He bringeth up clouds from the end of the earth: he hath made lightnings for the rain. He bringeth forth winds out of his stores:
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
He slew the firstborn of Egypt from man even unto beast.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
He sent forth signs and wonders in the midst of thee, O Egypt: upon Pharao, and upon all his servants.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
He smote many nations, and slew mighty kings:
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sehon king of the Amorrhites, and Og king of Basan, and all the kingdoms of Chanaan.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
And gave their land for an inheritance, for an inheritance to his people Israel.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Thy name, O Lord, is for ever: thy memorial, O Lord, unto all generations.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
For the Lord will judge his people, and will be entreated in favour of his servants.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
The idols of the Gentiles are silver and gold, the works of men’s hands.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
They have a mouth, but they speak not: they have eyes, but they see not.
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
They have ears, but they hear not: neither is there any breath in their mouths.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Let them that make them be like to them: and every one that trusteth in them.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Bless the Lord, O house of Israel: bless the Lord, O house of Aaron.
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Bless the Lord, O house of Levi: you that fear the Lord, bless the Lord.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Blessed be the Lord out of Sion, who dwelleth in Jerusalem.

< Masalimo 135 >