< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Hallelujah! Praise the name of Jehovah; praise, ye servants of Jehovah,
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
Ye that stand in the house of Jehovah, in the courts of the house of our God.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Praise ye Jah; for Jehovah is good: sing psalms unto his name; for it is pleasant.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
For Jah hath chosen Jacob unto himself, Israel for his own possession.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
For I know that Jehovah is great, and our Lord is above all gods.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Whatsoever Jehovah pleased, he hath done in the heavens and on the earth, in the seas and all deeps;
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
Who causeth the vapours to ascend from the ends of the earth; who maketh lightnings for the rain; who bringeth the wind out of his treasuries:
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
Who smote the firstborn of Egypt, both of man and beast;
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
Who sent signs and miracles into the midst of thee, O Egypt, upon Pharaoh and upon all his servants;
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Who smote great nations, and slew mighty kings,
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sihon king of the Amorites, and Og king of Bashan, and all the kingdoms of Canaan;
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
And gave their land for an inheritance, an inheritance unto Israel his people.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Thy name, O Jehovah, is for ever; thy memorial, O Jehovah, from generation to generation.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
For Jehovah will judge his people, and will repent in favour of his servants.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
The idols of the nations are silver and gold, the work of men's hands:
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
They have a mouth, and they speak not; eyes have they, and they see not;
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
They have ears, and they hear not; neither is there any breath in their mouth.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
They that make them are like unto them, — every one that confideth in them.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
House of Israel, bless ye Jehovah; house of Aaron, bless ye Jehovah;
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
House of Levi, bless ye Jehovah; ye that fear Jehovah, bless Jehovah.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Blessed be Jehovah out of Zion, who dwelleth at Jerusalem! Hallelujah!

< Masalimo 135 >