< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Alleluia. Praise the name of the Lord. You servants, praise the Lord.
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
You who stand in the house of the Lord, in the courts of the house of our God:
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
praise the Lord, for the Lord is good. Sing psalms to his name, for it is sweet.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
For the Lord has chosen Jacob for himself, Israel for his own possession.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
For I have known that the Lord is great, and our God is before all gods.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
All things whatsoever that he willed, the Lord did: in heaven, on earth, in the sea, and in all the deep places.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
He leads clouds from the ends of the earth. He has created lightnings in the rain. He has produced winds from his storehouses.
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
He struck the first-born of Egypt, from man even to cattle.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
He sent signs and wonders into your midst, O Egypt: upon Pharaoh and upon all his servants.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
He has struck many nations, and he has slaughtered strong kings:
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sihon, king of the Amorites, and Og, king of Bashan, and all the kingdoms of Canaan.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
And he gave their land as an inheritance, as an inheritance for his people Israel.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Your name, O Lord, is in eternity. Your memorial, O Lord, is from generation to generation.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
For the Lord will judge his people, and he will be petitioned by his servants.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
The idols of the Gentiles are silver and gold, the works of the hands of men.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
They have a mouth, and do not speak. They have eyes, and do not see.
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
They have ears, and do not hear. For neither is there any breath in their mouths.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Let those who make them become like them, along with all who trust in them.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Bless the Lord, O house of Israel. Bless the Lord, O house of Aaron.
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Bless the Lord, O house of Levi. You who fear the Lord, bless the Lord.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
The Lord is blessed from Zion, by those who dwell in Jerusalem.

< Masalimo 135 >