< Masalimo 135 >
1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
你们要赞美耶和华! 你们要赞美耶和华的名! 耶和华的仆人站在耶和华殿中; 站在我们 神殿院中的,你们要赞美他!
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
你们要赞美耶和华! 耶和华本为善; 要歌颂他的名, 因为这是美好的。
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
耶和华拣选雅各归自己, 拣选以色列特作自己的子民。
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
原来我知道耶和华为大, 也知道我们的主超乎万神之上。
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
耶和华在天上,在地下, 在海中,在一切的深处, 都随自己的意旨而行。
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
他使云雾从地极上腾, 造电随雨而闪, 从府库中带出风来。
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
他将埃及头生的, 连人带牲畜都击杀了。
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
埃及啊,他施行神迹奇事, 在你当中,在法老和他一切臣仆身上。
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
他击杀许多的民, 又杀戮大能的王,
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
就是亚摩利王西宏和巴珊王噩, 并迦南一切的国王,
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
将他们的地赏赐他的百姓以色列为业。
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
耶和华啊,你的名存到永远! 耶和华啊,你可记念的名存到万代!
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
耶和华要为他的百姓伸冤, 为他的仆人后悔。
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
外邦的偶像是金的,银的, 是人手所造的;
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
有口却不能言, 有眼却不能看,
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
有耳却不能听, 口中也没有气息。
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
造他的要和他一样, 凡靠他的也要如此。
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
以色列家啊,你们要称颂耶和华! 亚伦家啊,你们要称颂耶和华!
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
利未家啊,你们要称颂耶和华! 你们敬畏耶和华的,要称颂耶和华!
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
住在耶路撒冷的耶和华 该从锡安受称颂。 你们要赞美耶和华!