< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Pakai chu thangvah un! Pakai min chu thangvah un! Pakai lhacha ten Ama chu thang vah un,
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
nangho Pakai in a lhacha ten Pakai hongsung a in a chun.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Pakai chu aphatna jeh’in thangvah’un; amin ngaitah chu vahchoilan domsangun.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
Ajeh chu Pakai in Jacob chu Ama a dingmong monga alhen ahin, Israel chu atumbeh’a amagou dinga agon ahi.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Keiman Pakai aletna leh aloupina chu kahen, Ipakai uhi pathen dang sanga lenjo le loupijo ahi.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Pakai in van le leiset chunga hin, twikanglen thuh sunga hin aman alunglhaina a adeidei abol ahi.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
Aman meiho jonghi leiset chunga kon a alentousah ahin, Aman gojuh pet in koljong aphetsah’in, huijong hi athilkholna a kon in ahin lhadohjin ahi.
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
Aman Egypt te insunga chun ainson in mihemle ganhing jong apeng masa jouse ana sugam in ahi.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
Aman Egypt a chun Pharaoh le amipi jouse douna in datmo umtah thilkidangho ana tongdoh’in ahi.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Aman namlentah tah ho anavolhun leng thupi tahtah hojong ana ssatchap e.
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Amor lengpa Sihon, Bashan lengpa Og chuleh Caanan lengho jouse anathat gam in ahi.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
Aman agam u chu Ama goulo Israelte gamtum dingin anapen ahi.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
O Pakai namin hi tonsot'a umjing ding ahi.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
Ajehhcu Pakai in amite chunga thutah’a vaihom ding asohte chunga khotona aneiding ahi.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Chitin namtinte doilim hohi sana le dangka maimai mihem in asemthubou ahi.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Amahon kam anei un ima aseithei pouvin, mit anei un ima amuthei pouvin,
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
kol anei un ima ajathei pouvin nahkui anei un ima anahthei pouvin ahi.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Doilim semthu ho jouse le hiche tahsanho jouse chu hitobang ngen ahiuve.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Vo Israel Pakai chu thangvah’un! O thempu Aaron chilhahho, Pakai chu thangvah’un,
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
O Levite Pakai chu thangvah’un! Nangho Pakai ginna neijouse Pakai chu thangvah’un!
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Zion’a kon in Pakai chu thangvah’un ajeh chu Ama Jerusalema hin achengin ahi. Pakai chu thangvah’un!

< Masalimo 135 >