< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
BOEIPA te thangthen uh. BOEIPA ming te thangthen uh. BOEIPA kah sal rhoek thangthen uh.
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
Te rhoek tah mamih Pathen im vongup kah BOEIPA im ah pai uh.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
BOEIPA tah a then dongah BOEIPA mah thangthen uh. A ming te a naepnoi la tingtoeng uh.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
Jakob te BOEIPA amah ham, Israel khaw a lungthen la a coelh.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Kai loh YAHWEH neh mamih Boeipa tah Pathen boeih lakah len tila ka ming.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
BOEIPA loh a ngaih boeih te tah vaan ah khaw, diklai ah khaw, tuitunli neh tuidung khui boeih ah khaw a saii.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
Diklai khobawt lamkah khomong aka caeh sak loh rhaek neh khotlan khaw a saii tih a thakvoh khui lamkah khohli te a poh.
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
Amah loh Egypt hlang neh rhamsa caming rhoek te a ngawn.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
Miknoek neh kopoekrhai te namah Egypt khui ah khaw, Pharaoh taeng neh a sal rhoek boeih taengah khaw a tueih.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Amah loh namtom rhoek te muep a ngawn tih manghai boei rhoek khaw a ngawn.
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Amori manghai Sihon, Bashan manghai Oga neh Kanaan ram boeih te khaw a thup.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
Te dongah amih kah khohmuen rho te a pilnam Israel taengah rho la a paek.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
BOEIPA namah ming tah kumhal duela, BOEIPA namah poekkoepnah te cadilcahma phoeikah cadilcahma duela om pai saeh.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
BOEIPA loh a pilnam a tang sak vetih a sal rhoek te a hloep ni.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Namtom rhoek kah ngun neh sui muei he hlang kut bibi ni.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Amih kah a ka om dae cal uh thai pawh. A mik om uh dae hmu uh thai pawh.
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
A hna te om uh dae hnakaeng uh thai pawh. A ka khuiah khaw a hil om pawh.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Mueirhol aka saii neh amih dongah aka pangtung boeih tah mueirhol bangla om uh ni.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Israel imkhui loh BOEIPA te yoethen pae lah. Aaron imkhui loh BOEIPA te yoethen pae lah.
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Levi imkhui loh BOEIPA te yoethen pae lah. BOEIPA aka rhih rhoek loh BOEIPA te yoethen pae lah.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Zion lamloh BOEIPA te yoethen pae lah. Jerusalem kah khosa rhoek loh BOEIPA thangthen lah.

< Masalimo 135 >