< Masalimo 133 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!
En sang ved festreisene; av David. Se, hvor godt og hvor liflig det er at brødre også bor sammen!
2 Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu, otsikira ku ndevu, ku ndevu za Aaroni, oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.
Det er som den gode olje på hodet, som flyter ned på skjegget, Arons skjegg, som flyter ned på sømmen av hans klædebon,
3 Zili ngati mame a ku Heremoni otsikira pa Phiri la Ziyoni. Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso, ndiwo moyo wamuyaya.
Som Hermons-dugg, som flyter ned på Sions berg; for der har Herren satt velsignelsen, liv til evig tid.