< Masalimo 133 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!
Behold, how good and how pleasant it is for brothers to dwell together in unity!
2 Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu, otsikira ku ndevu, ku ndevu za Aaroni, oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.
It is like the precious oil upon the head, that ran down upon the beard, even Aaron's beard, that came down upon the skirt of his garments,
3 Zili ngati mame a ku Heremoni otsikira pa Phiri la Ziyoni. Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso, ndiwo moyo wamuyaya.
like the dew of Hermon, that comes down upon the mountains of Zion. For there Jehovah commanded the blessing, even life for evermore.

< Masalimo 133 >