< Masalimo 133 >
1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!
Sang til Festrejserne. Af David. Se, hvor godt og lifligt er det, naar Brødre bor tilsammen:
2 Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu, otsikira ku ndevu, ku ndevu za Aaroni, oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.
som kostelig Olie, der flyder fra Hovedet ned over Skægget, Arons Skæg, der bølger ned over Kjortelens Halslinning,
3 Zili ngati mame a ku Heremoni otsikira pa Phiri la Ziyoni. Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso, ndiwo moyo wamuyaya.
som Hermons Dug, der falder paa Zions Bjerge. Thi der skikker HERREN Velsignelse ned, Liv til evig Tid.