< Masalimo 132 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira.
Ɔsoroforo dwom. Awurade kae Dawid ne ɔhaw ahorow a ogyinaa ano no.
2 Iye analumbira kwa Yehova ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
Ɔkaa Awurade ntam, na ɔhyɛɛ nea ɔyɛ Otumfo ma Yakob no bɔ se,
3 “Sindidzalowa mʼnyumba mwanga kapena kugona pa bedi langa:
“Merenhyɛn me fi na merenkɔda me mpa so,
4 sindidzalola kuti maso anga agone, kapena zikope zanga ziwodzere,
meremma nna mmfa me na meremma mʼani nkum,
5 mpaka nditamupezera malo Yehova, malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”
kosi sɛ menya baabi ama Awurade, baabi a nea ɔyɛ Otumfo ma Yakob No bɛtena.”
6 Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata, tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
Yɛtee wɔ Efrata, yɛbɛtoo so wɔ Yaar mfuw so.
7 “Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo; tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
“Momma yɛnkɔ nʼatenae; momma yɛnsom wɔ ne nan ntiaso hɔ.
8 ‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira, Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
‘Awurade, sɔre bra wʼahomegyebea, wo ne wo tumi adaka no.
9 Ansembe anu avekedwe chilungamo; anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’”
Ma trenee nyɛ sɛ ntade mma wʼasɔfo; ma wʼahotefo nto ahurusi nnwom.’”
10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu, musakane wodzozedwa wanu.
Wo somfo Dawid nti, nyi wʼani mfi nea woasra no ngo no so.
11 Yehova analumbira kwa Davide, lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha: “Mmodzi wa ana ako ndidzamuyika pa mpando waufumu;
Awurade kaa ntam kyerɛɛ Dawid, nokware ntam a ɔntwe nsan se, “Wʼasefo no mu baako na mede no bɛtena wʼahengua so.
12 ngati ana ako azisunga pangano langa ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa, pamenepo ana awo adzakhala pa mpando wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”
Sɛ wo mmabarima di mʼapam so na wotie me nkyerɛkyerɛ a, ɛno de wɔn mmabarima bɛtena wʼahengua so afebɔɔ.”
13 Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
Awurade ayi Sion, ɔde hɔ ayɛ nʼatenae:
14 “Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi; ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
“Ɛha ne mʼahomegyebea daa nyinaa; ɛha na mɛtena adi hene, efisɛ ha na mepɛ,
15 Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri; anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
mede nneɛma pa bebree behyira no na mama nʼahiafo adidi amee.
16 Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.
Mede nkwagye befura nʼasɔfo, na nʼahotewfo ato ahurusi nnwom daa.
17 “Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
“Mɛma obirɛmpɔn bi apue wɔ Dawid ahenni mu, na mede kanea asi hɔ ama nea masra no ngo no.
18 Ndidzaveka adani ake manyazi, koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”
Mede aniwu befura nʼatamfo, nanso wɔbɛhyɛ no ahenkyɛw a ɛhyerɛn.”

< Masalimo 132 >