< Masalimo 132 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira.
Khumbula, Nkosi, uDavida, izinhlupheko zakhe zonke,
2 Iye analumbira kwa Yehova ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
ukuthi wafunga eNkosini, wathembisa kuSomandla kaJakobe:
3 “Sindidzalowa mʼnyumba mwanga kapena kugona pa bedi langa:
Qotho, kangiyikungena ethenteni lendlu yami, qotho, kangiyikwenyukela ecansini lombheda wami;
4 sindidzalola kuti maso anga agone, kapena zikope zanga ziwodzere,
qotho, kangiyikunika amehlo ami ubuthongo, ukuwozela ezinkopheni zami,
5 mpaka nditamupezera malo Yehova, malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”
ngize ngiyitholele iNkosi indawo, indawo zokuhlala uSomandla kaJakobe.
6 Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata, tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
Khangela, sakuzwa eEfratha, sakuthola emasimini egusu.
7 “Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo; tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
Sizangena ezindlini zayo zokuhlala, sikhonze esenabelweni senyawo zayo.
8 ‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira, Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
Sukuma, Nkosi, uye ekuphumuleni kwakho, wena lomtshokotsho wamandla akho!
9 Ansembe anu avekedwe chilungamo; anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’”
Abapristi bakho kabembeswe ukulunga, labangcwele bakho bathabe kakhulu.
10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu, musakane wodzozedwa wanu.
Ngenxa yenceku yakho uDavida ungafulathelisi ubuso bogcotshiweyo wakho.
11 Yehova analumbira kwa Davide, lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha: “Mmodzi wa ana ako ndidzamuyika pa mpando waufumu;
INkosi yafunga ngeqiniso kuDavida, kayiyikubuyela emuva kilo: Owesithelo sesizalo sakho ngizambeka esihlalweni sakho sobukhosi.
12 ngati ana ako azisunga pangano langa ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa, pamenepo ana awo adzakhala pa mpando wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”
Uba abantwana bakho begcina isivumelwano sami lezifakazelo zami engizabafundisa zona, labantwana babo bazahlala esihlalweni sakho sobukhosi kuze kube nini lanini.
13 Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
Ngoba iNkosi iyikhethile iZiyoni, iyifisile ibe yindawo yayo yokuhlala.
14 “Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi; ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
Le yindawo yami yokuphumula kuze kube nini lanini; lapha ngizahlala, ngoba ngiyifisile.
15 Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri; anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
Ngizabusisa kakhulu ukudla kwayo, ngisuthise abayanga bayo ngesinkwa.
16 Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.
Labapristi bayo ngizabembathisa usindiso, labangcwele bayo bazahlabelela kakhulu ngenjabulo.
17 “Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
Lapho ngizahlumisa uphondo lukaDavida; ngimisele ogcotshiweyo wami isibane.
18 Ndidzaveka adani ake manyazi, koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”
Izitha zakhe ngizazembathisa ihlazo, kodwa phezu kwakhe uzakhazimula umqhele wakhe wobukhosi.

< Masalimo 132 >