< Masalimo 132 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira.
성전에 올라가는 노래 여호와여 다윗을 위하여 그의 모든 근심한 것을 기억하소서
2 Iye analumbira kwa Yehova ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
저가 여호와께 맹세하며 야곱의 전능자에게 서원하기를
3 “Sindidzalowa mʼnyumba mwanga kapena kugona pa bedi langa:
내가 실로 나의 거하는 장막에 들어가지 아니하며 내 침상에 오르지 아니하며
4 sindidzalola kuti maso anga agone, kapena zikope zanga ziwodzere,
내 눈으로 잠들게 아니하며 내 눈꺼풀로 졸게 아니하기를
5 mpaka nditamupezera malo Yehova, malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”
여호와의 처소 곧 야곱의 전능자의 성막을 발견하기까지 하리라 하였나이다
6 Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata, tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
우리가 그것이 에브라다에 있다 함을 들었더니 나무 밭에서 찾았도다
7 “Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo; tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
우리가 그의 성막에 들어가서 그 발등상 앞에서 경배하리로다
8 ‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira, Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
여호와여 일어나사 주의 권능의 궤와 함께 평안한 곳으로 들어가소서
9 Ansembe anu avekedwe chilungamo; anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’”
주의 제사장들은 의를 입고 주의 성도들은 즐거이 외칠지어다
10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu, musakane wodzozedwa wanu.
주의 종 다윗을 위하여 주의 기름 받은 자의 얼굴을 물리치지 마옵소서
11 Yehova analumbira kwa Davide, lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha: “Mmodzi wa ana ako ndidzamuyika pa mpando waufumu;
여호와께서 다윗에게 성실히 맹세하셨으니 변치 아니하실지라 이르시기를 네 몸의 소생을 네 위에 둘지라
12 ngati ana ako azisunga pangano langa ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa, pamenepo ana awo adzakhala pa mpando wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”
네 자손이 내 언약과 저희에게 교훈하는 내 증거를 지킬진대 저희 후손도 영원히 네 위에 앉으리라 하셨도다
13 Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
여호와께서 시온을 택하시고 자기 거처를 삼고자 하여 이르시기를
14 “Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi; ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
이는 나의 영원히 쉴 곳이라 내가 여기 거할 것은 이를 원하였음이로다
15 Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri; anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
내가 이 성의 식료품에 풍족히 복을 주고 양식으로 그 빈민을 만족케 하리로다
16 Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.
내가 그 제사장들에게 구원으로 입히리니 그 성도들은 즐거움으로 외치리로다
17 “Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
내가 거기서 다윗에게 뿔이 나게 할 것이라 내가 내 기름 부은 자를 위하여 등을 예비하였도다
18 Ndidzaveka adani ake manyazi, koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”
내가 저의 원수에게는 수치로 입히고 저에게는 면류관이 빛나게 하리라 하셨도다

< Masalimo 132 >