< Masalimo 132 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira.
上行之詩。 耶和華啊,求你記念大衛所受的一切苦難!
2 Iye analumbira kwa Yehova ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
他怎樣向耶和華起誓, 向雅各的大能者許願,
3 “Sindidzalowa mʼnyumba mwanga kapena kugona pa bedi langa:
說:我必不進我的帳幕, 也不上我的床榻;
4 sindidzalola kuti maso anga agone, kapena zikope zanga ziwodzere,
我不容我的眼睛睡覺, 也不容我的眼目打盹;
5 mpaka nditamupezera malo Yehova, malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”
直等我為耶和華尋得所在, 為雅各的大能者尋得居所。
6 Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata, tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
我們聽說約櫃在以法他, 我們在基列‧耶琳就尋見了。
7 “Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo; tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
我們要進他的居所, 在他腳凳前下拜。
8 ‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira, Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
耶和華啊,求你興起, 和你有能力的約櫃同入安息之所!
9 Ansembe anu avekedwe chilungamo; anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’”
願你的祭司披上公義! 願你的聖民歡呼!
10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu, musakane wodzozedwa wanu.
求你因你僕人大衛的緣故, 不要厭棄你的受膏者!
11 Yehova analumbira kwa Davide, lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha: “Mmodzi wa ana ako ndidzamuyika pa mpando waufumu;
耶和華向大衛、憑誠實起了誓, 必不反覆,說: 我要使你所生的 坐在你的寶座上。
12 ngati ana ako azisunga pangano langa ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa, pamenepo ana awo adzakhala pa mpando wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”
你的眾子若守我的約 和我所教訓他們的法度, 他們的子孫必永遠坐在你的寶座上。
13 Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
因為耶和華揀選了錫安, 願意當作自己的居所,
14 “Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi; ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
說:這是我永遠安息之所; 我要住在這裏, 因為是我所願意的。
15 Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri; anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
我要使其中的糧食豐滿, 使其中的窮人飽足。
16 Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.
我要使祭司披上救恩, 聖民大聲歡呼!
17 “Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
我要叫大衛的角在那裏發生; 我為我的受膏者預備明燈。
18 Ndidzaveka adani ake manyazi, koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”
我要使他的仇敵披上羞恥; 但他的冠冕要在頭上發光。

< Masalimo 132 >