< Masalimo 132 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira.
Tangtlaeng Laa Aw BOEIPA David ham a phaep pah te boeih poek pah.
2 Iye analumbira kwa Yehova ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
BOEIPA taengah a caeng tih Jakob samrhang taengah khaw a caeng coeng.
3 “Sindidzalowa mʼnyumba mwanga kapena kugona pa bedi langa:
Ka dap im khuila ka pawk pawt vetih ka soengca rhaenghmuen khaw ka paan mahpawh.
4 sindidzalola kuti maso anga agone, kapena zikope zanga ziwodzere,
Ka mik te ih sak ham, ka mikkhu te ngam sak ham ka pae mahpawh.
5 mpaka nditamupezera malo Yehova, malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”
BOEIPA ham a hmuen neh Jakob kah samrhang ham tolhmuen ka hmuh duela.
6 Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata, tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
Khohmuen duup ah m'hmuh te Epharath ah khaw n'yaak uh coeng.
7 “Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo; tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
A tolhmuen la cet uh sih lamtah a kho kah khotloeng taengah bawk uh sih.
8 ‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira, Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
Aw BOEIPA nang na duemnah neh na sarhi thingkawng taengah thoo lah.
9 Ansembe anu avekedwe chilungamo; anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’”
Na khosoih rhoek loh duengnah bai uh saeh lamtah na hlangcim rhoek loh tamhoe uh saeh.
10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu, musakane wodzozedwa wanu.
Na sal David ham tah na koelh kah maelhmai te na mangthuung tak moenih.
11 Yehova analumbira kwa Davide, lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha: “Mmodzi wa ana ako ndidzamuyika pa mpando waufumu;
BOEIPA loh David taengah oltak la a caeng coeng. Na bungko thaihtae lamkah khaw te lamloh mael pawt vetih nang ham ngolkhoel soah kang khueh bitni.
12 ngati ana ako azisunga pangano langa ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa, pamenepo ana awo adzakhala pa mpando wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”
Ka paipi neh amih ka tukkil ka olphong te na ca rhoek loh a ngaithuen uh atah a ca rhoek khaw na ngolkhoel dongah a yoeyah la ngol uh ni.
13 Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
BOEIPA loh Zion te a coelh tih amah tolrhum la a sahnaih thil.
14 “Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi; ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
Ka duemnah he ka sahnaih coeng dongah a yoeyah la pahoi ka ngol thil ni.
15 Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri; anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
A sakah te ka uem ka uem pah vetih a khuikah khodaeng rhoek te buh ka cung sak ni.
16 Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.
Te vaengah a khosoih rhoek te khangnah ka bai sak vetih a hlangcim rhoek loh tamhoe la tamhoe uh ni.
17 “Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
David ham ki pahoi ka cawn sak vetih ka koelh ham hmaithoi ka tok pah ni.
18 Ndidzaveka adani ake manyazi, koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”
A thunkha rhoek te yahpohnah ka bai sak vetih anih te a rhuisam neh ka khooi sak ni.