< Masalimo 131 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide. Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza, maso anga siwonyada; sinditengeteka mtima ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
A Song of Ascents; of David. LORD, my heart is not haughty, nor mine eyes lofty; neither do I exercise myself in great matters, or in things too wonderful for me.
2 Koma moyo wanga ndawutontholetsa ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa, moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.
Surely I have stilled and quieted my soul; like a weaned child with his mother, my soul is with me like a weaned child.
3 Yembekeza Yehova, iwe Israeli, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
O Israel, hope in the LORD from this time forth and for evermore.

< Masalimo 131 >