< Masalimo 131 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide. Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza, maso anga siwonyada; sinditengeteka mtima ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
[A Song of Ascents. By David.] YHWH, my heart isn't haughty, nor my eyes lofty; nor do I concern myself with great matters, or things too wonderful for me.
2 Koma moyo wanga ndawutontholetsa ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa, moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.
Surely I have stilled and quieted my soul, like a weaned child with his mother, like a weaned child is my soul within me.
3 Yembekeza Yehova, iwe Israeli, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Israel, hope in YHWH, from this time forth and forevermore.

< Masalimo 131 >