< Masalimo 131 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Davide. Inu Yehova, mtima wanga siwodzikuza, maso anga siwonyada; sinditengeteka mtima ndi zinthu zapamwamba ndi zodabwitsa.
Yhwh, my heart is not haughty, nor mine eyes lofty: neither do I exercise myself in great matters, or in things too high for me.
2 Koma moyo wanga ndawutontholetsa ndi kuwukhalitsa chete ngati mwana amene amayi ake amuletsa kuyamwa, moyo wanga mʼkati mwanga uli ngati mwana amene amuletsa kuyamwa.
Surely I have behaved and quieted myself, as a child that is weaned of his mother: my soul is even as a weaned child.
3 Yembekeza Yehova, iwe Israeli, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Let Israel hope in Yhwh from henceforth and for ever.