< Masalimo 130 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikulirira kwa Inu Yehova ndili mʼdzenje lozama;
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikulirira kwa Inu Yehova ndili mʼdzenje lozama;
2 Ambuye imvani mawu anga. Makutu anu akhale tcheru kumva kupempha chifundo kwanga.
Ambuye imvani mawu anga. Makutu anu akhale tcheru kumva kupempha chifundo kwanga.
3 Inu Yehova, mukanamawerengera machimo, Inu Yehova, akanayima chilili ndani wopanda mlandu?
Inu Yehova, mukanamawerengera machimo, Inu Yehova, akanayima chilili ndani wopanda mlandu?
4 Koma kwa Inu kuli chikhululukiro; nʼchifukwa chake mumaopedwa.
Koma kwa Inu kuli chikhululukiro; nʼchifukwa chake mumaopedwa.
5 Ndimayembekezera Yehova, moyo wanga umayembekezera, ndipo ndimakhulupirira mawu ake.
Ndimayembekezera Yehova, moyo wanga umayembekezera, ndipo ndimakhulupirira mawu ake.
6 Moyo wanga umayembekezera Ambuye, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa, inde, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,
Moyo wanga umayembekezera Ambuye, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa, inde, kupambana momwe alonda amayembekezera mmawa,
7 Yembekeza Yehova, iwe Israeli, pakuti Yehova ali ndi chikondi chosasinthika ndipo alinso ndi chipulumutso chochuluka.
Yembekeza Yehova, iwe Israeli, pakuti Yehova ali ndi chikondi chosasinthika ndipo alinso ndi chipulumutso chochuluka.
8 Iye mwini adzawombola Israeli ku machimo ake onse.
Iye mwini adzawombola Israeli ku machimo ake onse.

< Masalimo 130 >