< Masalimo 13 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
Kumqondisi wokuhlabela. Ihubo likaDavida. Koze kube nini, Oh Thixo? Uzangikhohlwa lanininini na? Koze kube nini ungifihlela ubuso bakho na?
2 Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
Koze kube nini ngitshukumisana lemicabango yami, inhliziyo yami ihlale idabukile insuku zonke na? Koze kube nini isitha sami sitshakala phezu kwami?
3 Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
Ngizwela ungiphendule, Oh Thixo Nkulunkulu wami. Khanyisela amehlo ami funa ngihle ngilale kokuphela;
4 mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
isitha sami sizakuthi, “Sengimehlule,” labangizondayo bathokoze nxa ngisiwa.
5 Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
Kodwa ngiyalwethemba uthando lwabo olungapheliyo; inhliziyo yami iyathokoza ngensindiso yakho.
6 Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.
Ngizahlabelela kuThixo, ngoba ungenzele ukulunga.