< Masalimo 13 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
Psalmus David, in finem. Usquequo Domine oblivisceris me in finem? Usquequo avertis faciem tuam a me?
2 Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
Quamdiu ponam consilia in anima mea, dolorem in corde meo per diem?
3 Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
Usquequo exaltabitur inimicus meus super me?
4 mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
respice, et exaudi me Domine Deus meus. Illumina oculos meos ne umquam obdormiam in morte:
5 Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
ne quando dicat inimicus meus: Praevalui adversus eum. Qui tribulant me, exultabunt si motus fuero:
6 Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.
ego autem in misericordia tua speravi. Exultabit cor meum in salutari tuo: cantabo Domino qui bona tribuit mihi: et psallam nomini Domini altissimi.

< Masalimo 13 >