< Masalimo 13 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
To the Overseer. — A Psalm of David. Till when, O Jehovah, Dost Thou forget me? — for ever? Till when dost Thou hide Thy face from me?
2 Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
Till when do I set counsels in my soul? Sorrow in my heart daily? Till when is mine enemy exalted over me?
3 Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
Look attentively; Answer me, O Jehovah, my God, Enlighten mine eyes, lest I sleep in death,
4 mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
Lest mine enemy say, 'I overcame him,' Mine adversaries joy when I am moved.
5 Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
And I, in Thy kindness I have trusted, Rejoice doth my heart in Thy salvation.
6 Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.
I do sing to Jehovah, For He hath conferred benefits upon me!

< Masalimo 13 >