< Masalimo 13 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
To the chief Musician, A Psalm of David. How long wilt thou forget me, O LORD? for ever? how long wilt thou hide thy face from me?
2 Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
How long shall I take counsel in my soul, having sorrow in my heart daily? how long shall my enemy be exalted over me?
3 Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
Consider and hear me, O LORD my God: enlighten my eyes, lest I sleep the sleep of death;
4 mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
Lest my enemy say, I have prevailed against him; and those that trouble me rejoice when I am moved.
5 Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
But I have trusted in thy mercy; my heart shall rejoice in thy salvation.
6 Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.
I will sing to the LORD, because he hath dealt bountifully with me.

< Masalimo 13 >