< Masalimo 13 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
To him that excelleth. A Psalme of Dauid. Howe long wilt thou forget me, O Lord, for euer? howe long wilt thou hide thy face from me?
2 Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
How long shall I take counsell within my selfe, hauing wearinesse dayly in mine heart? how long shall mine enemie be exalted aboue me?
3 Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
Beholde, and heare mee, O Lord my God: lighten mine eyes, that I sleepe not in death:
4 mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
Lest mine enemie say, I haue preuailed against him: and they that afflict me, reioyce when I slide.
5 Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
But I trust in thy mercie: mine heart shall reioyce in thy saluation:
6 Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.
I will sing to the Lord, because he hath delt louingly with me.