< Masalimo 13 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
To the chief Musician. A Psalm of David. How long, Jehovah, wilt thou forget me for ever? how long wilt thou hide thy face from me?
2 Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
How long shall I take counsel in my soul, with sorrow in my heart daily? how long shall mine enemy be exalted over me?
3 Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
Consider, answer me, O Jehovah my God! lighten mine eyes, lest I sleep the [sleep of] death;
4 mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
Lest mine enemy say, I have prevailed against him! [lest] mine adversaries be joyful when I am moved.
5 Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
As for me, I have confided in thy loving-kindness; my heart shall be joyful in thy salvation.
6 Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.
I will sing unto Jehovah, for he hath dealt bountifully with me.

< Masalimo 13 >