< Masalimo 13 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale? Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
For the Chief Musician. A Psalm by David. How long, LORD? Will you forget me forever? How long will you hide your face from me?
2 Ndidzalimbana ndi maganizo anga ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti? Mpaka liti adani anga adzandipambana?
How long shall I take counsel in my soul, having sorrow in my heart every day? How long shall my enemy triumph over me?
3 Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga. Walitsani maso anga kuti ndingafe;
Behold, and answer me, LORD, my God. Give light to my eyes, lest I sleep in death;
4 mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,” ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
lest my enemy say, “I have prevailed against him;” lest my adversaries rejoice when I fall.
5 Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika; mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
But I trust in your loving kindness. My heart rejoices in your salvation.
6 Ine ndidzayimbira Yehova pakuti wandichitira zokoma.
I will sing to the LORD, because he has been good to me.

< Masalimo 13 >