< Masalimo 129 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
Canticum graduum. Saepe expugnaverunt me a iuventute mea, dicat nunc Israel.
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
Saepe expugnaverunt me a iuventute mea: etenim non potuerunt mihi.
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
Supra dorsum meum fabricaverunt peccatores: prolongaverunt iniquitatem suam.
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
Dominus iustus concidet cervices peccatorum:
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
confundantur et convertantur retrorsum omnes, qui oderunt Sion.
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
Fiant sicut foenum tectorum: quod priusquam evellatur, exaruit:
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
De quo non implebit manum suam qui metit, et sinum suum qui manipulos colligit.
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
Et non dixerunt qui praeteribant: Benedictio Domini super vos: benediximus vobis in nomine Domini.

< Masalimo 129 >