< Masalimo 129 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
१यात्रा का गीत इस्राएल अब यह कहे, “मेरे बचपन से लोग मुझे बार बार क्लेश देते आए हैं,
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
२मेरे बचपन से वे मुझ को बार बार क्लेश देते तो आए हैं, परन्तु मुझ पर प्रबल नहीं हुए।
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
३हलवाहों ने मेरी पीठ के ऊपर हल चलाया, और लम्बी-लम्बी रेखाएँ की।”
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
४यहोवा धर्मी है; उसने दुष्टों के फंदों को काट डाला है;
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
५जितने सिय्योन से बैर रखते हैं, वे सब लज्जित हों, और पराजित होकर पीछे हट जाए!
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
६वे छत पर की घास के समान हों, जो बढ़ने से पहले सूख जाती है;
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
७जिससे कोई लवनेवाला अपनी मुट्ठी नहीं भरता, न पूलियों का कोई बाँधनेवाला अपनी अँकवार भर पाता है,
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
८और न आने-जानेवाले यह कहते हैं, “यहोवा की आशीष तुम पर होवे! हम तुम को यहोवा के नाम से आशीर्वाद देते हैं!”