< Masalimo 129 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
Cantique des degrés. "Violemment on m’a persécuté dès ma jeunesse peut bien dire Israël
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
violemment on m’a persécuté dès ma jeunesse, mais on n’a pu triompher de moi.
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
Des laboureurs ont labouré mon dos, y ont tracé de longs sillons."
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
L’Eternel est juste, il brise les entraves des méchants.
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
Qu’ils rougissent et reculent, tous ceux qui haïssent Sion!
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
Qu’ils soient comme l’herbe des toits, qui se dessèche avant qu’on l’enlève,
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
dont le moissonneur n’emplit pas sa main, ni le faiseur de gerbes son giron!
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
De sorte que les passants ne disent point: "La bénédiction de Dieu soit sur vous! Nous vous bénissons au nom de l’Eternel."

< Masalimo 129 >