< Masalimo 129 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
Une chanson d'ascension. Ils m'ont souvent affligé depuis ma jeunesse. Laissez Israël dire maintenant:
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
maintes fois ils m'ont affligé depuis ma jeunesse, mais ils n'ont pas prévalu contre moi.
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
Les laboureurs ont labouré sur mon dos. Ils ont tracé de longs sillons.
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
Yahvé est juste. Il a coupé les cordes des méchants.
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
Qu'ils soient déçus et retournent en arrière, tous ceux qui détestent Sion.
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
Qu'ils soient comme l'herbe sur les toits, qui se fane avant de grandir,
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
avec lesquels la faucheuse ne remplit pas sa main, ni celui qui lie les gerbes, sa poitrine.
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
Et ceux qui passent ne disent pas non plus, « Que la bénédiction de Yahvé soit sur vous. Nous vous bénissons au nom de Yahvé. »