< Masalimo 129 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
A song of ascents. “Often since my youth they have attacked me,” let Israel say.
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
“Often since my youth they have attacked me, yet they have not defeated me.
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
The plowers plowed on my back; they made their furrows long.
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
Yahweh is righteous; he has cut the ropes of the wicked.”
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
May they all be put to shame and turned back, those who hate Zion.
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
May they be like the grass on the housetops that withers before it grows up,
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
that cannot fill the reaper's hand or the chest of the one who binds bundles of grain together.
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
May those who pass by not say, “May the blessing of Yahweh be on you; we bless you in the name of Yahweh.”