< Masalimo 129 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
Many times they have afflicted me from my youth up. Let Israel [God prevails] now say,
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
many times they have afflicted me from my youth up, yet they have not prevailed against me.
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
The plowers plowed on my back. They made their furrows long.
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
Adonai is righteous. He has cut apart the cords of the wicked.
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
Let them be disappointed and turned backward, all those who hate Zion [Mountain ridge, Marking].
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
Let them be as the grass on the housetops, which withers before it grows up;
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
with which the reaper does not fill his hand, nor he who binds sheaves, his bosom.
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
Neither do those who go by say, “The blessing of Adonai be on you. We bless you in Adonai’s name.”