< Masalimo 129 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
“A psalm of the steps, or the goings up.” Much have they afflicted me from my youth, May Israel now say;
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
Much have they afflicted me from my youth, Yet have they not prevailed against me.
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
The ploughers ploughed up my back; They made long their furrows;
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
But the LORD was righteous; He cut asunder the cords of the wicked.
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
Let all be driven back with shame Who hate Zion!
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
Let them be as grass upon the house-tops, Which withereth before one pulleth it up;
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
With which the reaper filleth not his hand, Nor he that bindeth sheaves his bosom!
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
And they who pass by do not say, “The blessing of the LORD be upon you! We bless you in the name of the LORD!”