< Masalimo 129 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
A song of degrees. They haue often times afflicted me from my youth (may Israel nowe say)
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
They haue often times afflicted me from my youth: but they could not preuaile against me.
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
The plowers plowed vpon my backe, and made long furrowes.
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
But the righteous Lord hath cut the cordes of the wicked.
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
They that hate Zion, shalbe all ashamed and turned backward.
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
They shalbe as the grasse on the house tops, which withereth afore it commeth forth.
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
Whereof the mower filleth not his hand, neither the glainer his lap:
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
Neither they, which go by, say, The blessing of the Lord be vpon you, or, We blesse you in the Name of the Lord.