< Masalimo 129 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
A Canticle in steps. They have often fought against me from my youth, let Israel now say:
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
they have often fought against me from my youth, yet they could not prevail over me.
3 Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
The sinners have made fabrications behind my back. They have prolonged their iniquity.
4 Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
The just Lord will cut the necks of sinners.
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
Let all those who hate Zion be confounded and turned backwards.
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
Let them be like grass on the rooftops, which withers before it can be pulled up:
7 sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
with it, he who reaps does not fill his hand and he who gathers sheaves does not fill his bosom.
8 Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
And those who were passing by have not said to them: “The blessing of the Lord be upon you. We have blessed you in the name of the Lord.”

< Masalimo 129 >