< Masalimo 128 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
Ɔsoroforo dwom. Nhyira ne wɔn a wosuro Awurade, na wɔnantew nʼakwan so.
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
Wubedi wʼadwuma so aba; nhyira ne yiyedi bɛyɛ wo de.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Wo yere bɛyɛ sɛ bobe a ɛsow aba wɔ wo fi; na wo mmabarima ayɛ sɛ ngodua a afifi atwa wo pon ho ahyia.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Yiw, sɛɛ ne nea wobehyira onipa a osuro Awurade no.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
Awurade nhyira wo mfi Sion na ɔmma wunhu Yerusalem yiyeyɛ; wo nkwanna nyinaa.
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
Ɔmma wo ntena ase nhu wo mma mma. Asomdwoe nka Israel.

< Masalimo 128 >