< Masalimo 128 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
Blagoslovljen je vsak, kdor se boji Gospoda, ki hodi po njegovih poteh.
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
Kajti jedel boš trud svojih rok, srečen boš in s teboj bo dobro.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Tvoja žena bo kakor rodovitna trta ob straneh tvoje hiše; tvoji otroci kakor oljčne sadike naokrog tvoje mize.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Glej, tako bo blagoslovljen mož, ki se boji Gospoda.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
Gospod naj te blagoslovi iz Siona in gledal boš dobro Jeruzalema vse dni svojega življenja.
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
Da, videl boš svojih otrok otroke in mir nad Izraelom.

< Masalimo 128 >