< Masalimo 128 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
Canticum graduum. Beati omnes, qui timent Dominum, qui ambulant in viis eius.
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
Labores manuum tuarum quia manducabis: beatus es, et bene tibi erit.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Uxor tua sicut vitis abundans, in lateribus domus tuae. Filii tui sicut novellae olivarum, in circuitu mensae tuae.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Ecce sic benedicetur homo, qui timet Dominum.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
Benedicat tibi Dominus ex Sion: et videas bona Ierusalem omnibus diebus vitae tuae.
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
Et videas filios filiorum tuorum, pacem super Israel.

< Masalimo 128 >