< Masalimo 128 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
The song of greces. Blessid ben alle men, that dreden the Lord; that gon in hise weies.
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
For thou schalt ete the trauels of thin hondis; thou art blessid, and it schal be wel to thee.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Thi wijf as a plenteous vyne; in the sidis of thin hous. Thi sones as the newe sprenges of olyue trees; in the cumpas of thi bord.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Lo! so a man schal be blessid; that dredith the Lord.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
The Lord blesse thee fro Syon; and se thou the goodis of Jerusalem in alle the daies of thi lijf.
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
And se thou the sones of thi sones; se thou pees on Israel.

< Masalimo 128 >