< Masalimo 128 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
A song of ascents. Blessed is everyone who honors Yahweh, who walks in his ways.
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
What your hands provide, you will enjoy; you will be blessed and prosper.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Your wife will be like a fruitful vine in your house; your children will be like olive plants as they sit around your table.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Yes, indeed, the man will be blessed who honors Yahweh.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
May Yahweh bless you from Zion; may you see the prosperity of Jerusalem all the days of your life.
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
May you live to see your children's children. May peace be on Israel.

< Masalimo 128 >