< Masalimo 128 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
A Song of Ascents. How happy is every one that revereth Yahweh, who walketh in his ways!
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
The labour of thine own hands, surely thou shalt eat. How happy thou, and well for thine!
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Thy wife, like a fruitful vine, within the recesses of thy house, —Thy children, like plantings of olive-trees, round about thy table.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Lo! thus, shall be blessed the man who revereth Yahweh.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
Yahweh will bless thee, out of Zion, —and behold thou the welfare of Jerusalem, all the days of thy life!
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
And behold thou thy children’s children, —Prosperity on Israel!

< Masalimo 128 >