< Masalimo 128 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
A SONG OF THE ASCENTS. O the blessedness of everyone fearing YHWH, Who is walking in His ways.
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
You surely eat the labor of your hands, You [are] blessed, and good [is] to you.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Your wife [is] as a fruitful vine in the sides of your house, Your sons as olive plants around your table.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Behold, surely thus is the man blessed who is fearing YHWH.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
YHWH blesses you out of Zion, Look, then, on the good of Jerusalem, All the days of your life,
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
And see the sons of your sons! Peace on Israel!

< Masalimo 128 >