< Masalimo 128 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
A Song of degrees. Blessed is every one that feareth Jehovah, that walketh in his ways.
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
For thou shalt eat the labour of thy hands; happy shalt thou be, and it shall be well with thee.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Thy wife shall be as a fruitful vine in the inner part of thy house; thy children like olive-plants round about thy table.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Behold, thus shall the man be blessed that feareth Jehovah.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
Jehovah will bless thee out of Zion; and mayest thou see the good of Jerusalem all the days of thy life,
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
And see thy children's children. Peace be upon Israel!

< Masalimo 128 >