< Masalimo 128 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
Lyksalig hver den, som frygter Herren, som gaar paa hans Veje!
2 Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
Thi du skal æde Frugten af dine Hænders Arbejde; lyksalig er du, og det gaar dig vel.
3 Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
Din Hustru er som et frugtbart Vintræ paa Siderne af dit Hus, dine Børn som Oliekviste omkring dit Bord.
4 Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
Se, saaledes skal den Mand velsignes, som frygter Herren.
5 Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
Herren skal velsigne dig fra Zion, og du skal se Jerusalems Lykke alle dit Livs Dage.
6 ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.
Og du skal se Børn af dine Børn! Fred være over Israel!