< Masalimo 127 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
Un chant d'ascension. Par Solomon. A moins que Yahvé ne construise la maison, ceux qui la construisent travaillent en vain. A moins que Yahvé ne veille sur la ville, le gardien la surveille en vain.
2 Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
C'est en vain que tu te lèves tôt, pour se coucher tard, en mangeant le pain du labeur, car il donne le sommeil à ses proches.
3 Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
Voici, les enfants sont un héritage de Yahvé. Le fruit de ses entrailles est sa récompense.
4 Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
Comme des flèches dans la main d'un homme puissant, Il en va de même pour les enfants de la jeunesse.
5 Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.
Heureux l'homme qui en a plein son carquois. Ils ne seront pas déçus lorsqu'ils parleront avec leurs ennemis à la porte.

< Masalimo 127 >