< Masalimo 127 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
A Song of Ascents. By Solomon. Unless the LORD builds the house, they who build it labour in vain. Unless the LORD watches over the city, the watchman guards it in vain.
2 Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
It is vain for you to rise up early, to stay up late, eating the bread of toil, for he gives sleep to his loved ones.
3 Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
Behold, children are a heritage of the LORD. The fruit of the womb is his reward.
4 Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
As arrows in the hand of a mighty man, so are the children of youth.
5 Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.
Happy is the man who has his quiver full of them. They won’t be disappointed when they speak with their enemies in the gate.

< Masalimo 127 >