< Masalimo 127 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
A Song of degrees for Solomon. Except the LORD shall build the house, they labour in vain that build it: except the LORD shall keep the city, the watchman waketh in vain.
2 Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
It is vain for you to rise early, to sit up late, to eat the bread of sorrows: for so he giveth his beloved sleep.
3 Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
Lo, children are an heritage of the LORD: and the fruit of the womb is his reward.
4 Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
As arrows are in the hand of a mighty man; so are children of the youth.
5 Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.
Happy is the man that hath his quiver full of them: they shall not be ashamed, but they shall speak with the enemies in the gate.

< Masalimo 127 >