< Masalimo 127 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
song [the] step to/for Solomon if: until LORD not to build house: home vanity: vain to toil to build him in/on/with him if: until LORD not to keep: guard city vanity: vain to watch to keep: guard
2 Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
vanity: vain to/for you to rise to arise: rise to delay to dwell to eat food: bread [the] toil so to give: give to/for beloved his sleep
3 Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
behold inheritance LORD son: child wages fruit [the] belly: womb
4 Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
like/as arrow in/on/with hand mighty man so son: child [the] youth
5 Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.
blessed [the] great man which to fill [obj] quiver his from them not be ashamed for to speak: speak with enemy in/on/with gate