< Masalimo 127 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
A Song of Ascents; of Solomon. Except the LORD build the house, they labour in vain that build it: except the LORD keep the city, the watchman waketh but in vain.
2 Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
It is vain for you that ye rise up early, and so late take rest, and eat the bread of toil: [for] so he giveth unto his beloved sleep.
3 Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
Lo, children are an heritage of the LORD: [and] the fruit of the womb is [his] reward.
4 Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
As arrows in the hand of a mighty man, so are the children of youth.
5 Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.
Happy is the man that hath his quiver full of them: they shall not be ashamed, when they speak with their enemies in the gate.

< Masalimo 127 >